20/04/2026
PANG’ONO NDI ZAMBIRI NGATI MULUNGU ALI MKATI
Mose ndi Ndodo Yake
Mulungu anaitana Mose kuti akakumane ndi munthu wamphamvu kwambiri padziko lonse lapansi (Farao) ndi kumasula mtundu wonse mu ukapolo. Koma Mose anali ndi zifukwa zambiri zozengereza. Mulungu sanatsutsane naye, koma anangofunsa funso limodzi: "Kodi m’dzanja mwako muli chiyani?" (Eksodo 4:2). Kwa Mose, inali ndodo chabe yoyang’anira nkhosa. Koma m’manja mwa Mulungu, ndodo yomweyo inapatula nyanja, kutulutsa madzi pathanthwe, ndi kuchita zozizwitsa pamaso pa Farao. Mulungu sankafuna kuti Mose akhale ndi zambiri; anafuna kuti Mose apereke chimene anali nacho kale.
Mkazi Wamasiye wa ku Zarefati
Mayi uyu anali atatsala ndi ufa wochepa kwambiri m’mbiya ndi mafuta pang’ono m’botolo. Anali kukonza chakudya chomaliza kuti adye ndi mwana wake asanafe ndi njala. Pa nthawi ya mavuto oterewa, Eliya anafika ndipo anamupempha kuti amudyetse choyamba. Mayiyu anamvera, ndipo kuyambira tsiku limenelo, ufa m’mbiya sunathe ndipo mafuta m’botolo sanaphwe mpaka pamene Mulungu anatumiza mvula ndipo chilala chinatha. (1 Mafumu 17:12-16).
Mafuta a Mkazi Wamasiye
Mayi wamasiye wina anali ndi ngongole ndipo ana ake anali pafupi kutengedwa kukhala akapolo. Elisa anamufunsa zimene anali nazo m’nyumba, ndipo anayankha kuti "palibe kalikonse, kupatula mtsuko wa mafuta." Eliya anamuuza kuti akatenge mitsuko yambiri yopanda kanthu n’kuyamba kuthira mafutawo. Mafutawo anapitiriza kutuluka mpaka mitsuko yonse inadzaza. Anagulitsa mafutawo, nalipira ngongole, ndipo ndalama zina zinatsala zoti amagwiritsira ntchito pa moyo wawo. (2 Mafumu 4:1-7).
Mnyamata Ndi Mikate Ndi Nsomba
Yesu anagwiritsa ntchito chakudya cha mnyamata wamng’ono—mikate isanu ndi nsomba ziwiri—kudyetsa khamu la anthu masauzande ambiri. Ngakhale zinkaoneka ngati sizingatheke, Yesu anachita chozizwitsa. Aliyense anadya n’kukhuta, ndipo zotsala zinadzaza madengu khumi ndi awiri. (Yohane 6:9-13).
Kobiri la Mkazi Wamasiye
Yesu anali m’kachisi akuyang’ana anthu akupereka chopereka. Olemera anaponya ndalama zambiri. Koma anaona mkazi wamasiye wosauka amene anaponya makobiri awiri ang’onoang’ono, amene analibe mtengo waukulu. Koma Yesu anauza ophunzira Ake kuti mayiyu wapereka kwambiri kuposa aliyense, chifukwa wapereka zonse zimene anali nazo. (Marko 12:41-44).
Anthu onsewa anali ndi chinthu chimodzi chofanana: Sanadikire mpaka atakhala ndi zambiri. Anapereka chimene anali nacho, pa nthawi imene anali nacho, ndipo anakhulupirira Mulungu pa zotsala zonse.
Chozizwitsa sichinadalire pa kuchuluka kwa chuma, koma pa kumvera. Mulungu sakufuna kuti mukhale ndi zambiri kaye kuti asonyeze mphamvu Yake. Akungofuna kuti mumukhulupirire ndi zimene muli nazo kale.
Ngati uthenga uwu wakulimbikitsani, tumizani kwa ena (repost).