Thupa CCAP Youth Nkhoma Synod

Thupa CCAP Youth Nkhoma Synod Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Thupa CCAP Youth Nkhoma Synod, Religious organisation, Kakonje Presbytery, Kasungu.

Kufalitsa uthenga wa Ambuye posayang'ana mtundu, chuma, komaso mtunda ndizina zambiri , koma kukwanilitsa mau a Ambuye omwe akuti pitani, kalalikileni KWA amitundu yonse

29/10/2025


Abale ndabwera ndinkhani yokwiyitsa.
Ndangomaliza kuyankhula ndi Mayi ku MILEPA kuja pa telephone.

Akuti mtumiki wina ataona kuti tinakapemphera nawo ,nayenso anapita(sizoletsedwa) koma chomvetsa Chisoni ndi choti anawakakamiza kuti ayime atamaliza mapemphero awo ,mpakana anawawongola mwendo ndikuthyoka ndipo ndikunena pano amayi aja ali mu ululu ndipo awaika chikhakha ndipo awagoneka ku Chipatala cha Chiradzulo.

Anthu a Mulungu anzanga, chonde mukapemphera ndi munthu , gwiritsani ntchito nzeru .Sibwino kumukakamiza munthu yemwe akudwala kuti achite zinthu zomwe sanachitepo nthawi yaitali. Nthawi zambiri thupi limakhala silinalandire mphamvu.

Mukawerenga mu Baibulo pa MACHITIDWE 3, munthu yemwe anali pa Kachisi uja anachita kumuthandizira kuti adzuke koma sanamukakamize kuti ayende.

Kupempherera anthu kumafunikanso chidziwitso ( knowledge of the word of God) komanso chikhulupiriro cha munthu mwini wake.

Sindikudziwa kuti anapita ndi ndani koma Ngati mukuwerenga Post iyi simunachite bwino kuwakakamiza kuti ayende. Nanga tamvani munthu wathyoka Bondo kamba kokakamizidwa ndi munthu wa Mulungu kuti ayime, thupi lawo linali lisanalimbe.

Pali machiritso ena amabwera pang'ono pang'ono ( Gradual Healing). Especially kwa omwe akhala akudwala nthawi yaitali.

Unfortunately amayiwo akuti sakumudziwa dzina lake mtumikiyu koma ananena kuti anawadziwa kudzera pa Facebook ,chifukwa choti tinapitako nkukapemphera nawo

Zandiwawa chifukwa amayiwa anachira kale titapemphera nawo muja ndipo amatha kukhala pansi bwinobwino.

Mulibwanji anthu okondeledwa ndi Yehova, nanga mpingo WA Ambuye ukuyenda bwanji
29/10/2025

Mulibwanji anthu okondeledwa ndi Yehova, nanga mpingo WA Ambuye ukuyenda bwanji

03/09/2025

Fanuel 'Billy' Mwale

03/09/2025

31/08/2025

Big shout out to my newest top fans! Fanuel 'Billy' Mwale

31/08/2025

Lero pa 31/8/2025 abusa a Rev Francis Mnkumbila anali kumatu zone komwe amakadyetsa mgonelo wa Ambuye ndipo analalikila mawu ochokera pa Genesis chapter 3-1-17

Mawu akulu anali pakuchimwa kwake kwamunthu

Abusawa anati ambiri takopeka ndiziphunzitso zina zatsopano ndipo tataya njila yake yomwe Mulungu aduna kuti anthu ake tidzichita tsiku ndi tsiku,

Munthu wa Mulunguyu anapitiliza kuti monga Adam ndi Hava adachitila kukavala, ndikubisala kuzitsamba chomwechoso lero ambiri akuchitabe zokhulupilira zitsamba, koteloso anati aliyense ochita zitsamba oteleyu adachoka pamaso pa YEHOVA,

Abusa popitiloza anena kuti akhristu ambiri amasiya kukhulupilira kuti mnkati mwapemhero muja muliyankho ndipo amapita kwaena amene adavala maonekedwe ngati mwana wankhosa namawafunsa kuti awanenelele zatsogolo lawo,

Munthu wa YEHOVA pochenjeza wati ngakhale titakumana ndi munthu wowoneka kuti wanyamula Bible mmanja namayenda kumaimba nyimbo za Mulungu, otelewa asatichotse pachikhulupiliro chathu chomwe tilinacho pa YEHOVA popeza ena otelewa ndiasing'anga,

Mulungu akudalitseni nonse chifukwa chakuwelenga uthenga wabwinowu,
Pangani share kwa anzanu komaso kugulupu ena
Olemba ndine Lovemore Guwende Ambuye akudalitseni zikomo🙏🙏🙏

16/09/2022

ZINAFIKA POKOKA MANJA KUNO KUNKHAMENYA CCAP MAKA KWA ANYAMATA ATHUPA CCAP POMWE ANALINKUFUSIDWA NDALAMA NDIBUNGWE LA PRESBYTERY, IZI ZINAKHUMUDWITSA ACHINYAMATA ATHUPA CCAP POMWE ANAGANIZA ZOBWELERA OSAPITILIZA NAWO MSONKHANO , IZI ZINADZA POPEZA ANALI AKUFUSIDWA NDALAMA YOKWANA 15 PIN YA ANTHU ATATU KAMBA KAKUTI ANAIGWILITSA NTCHITO NGAT TRANSPORT CHIFUKWA GALIMOTO YOMWE ANATENGA INAPANGA BREAKDOWN, KENAKO ANATENGA INA CHONCHO ZINADZETSA MPUNGWE PUNGWE POPEZA GALIMOTO YOYAMBAYO ANATCHAJA NTENGO WA FAIR KUSIYANA NDIYACHIWIRIYI, KOMA NDIKUNENA PANO ZONSE ZILIBWINO AKAMBILANA NDIPO PALIKUNVANA

ACHINYAMATA TINSE ATHUPA CCAP LERO TIKUNYAMUKA ULENDO WAKUNSONKHANO WAUKULU OMWE TIKACHITILE PA NKHAMENYA CCAP PAMODZI N...
15/09/2022

ACHINYAMATA TINSE ATHUPA CCAP LERO TIKUNYAMUKA ULENDO WAKUNSONKHANO WAUKULU OMWE TIKACHITILE PA NKHAMENYA CCAP PAMODZI NDIMIPINGO INA MONGA CHIZUNGU CCAP , NKHAMENYA CCAP, KAKONJE CCAP, JENDA CCAP , DWANGWA CCAP, TIYENI TONSE TIKAKUMANE KUMENEKO

Address

Kakonje Presbytery
Kasungu

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Thupa CCAP Youth Nkhoma Synod posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share