29/10/2025
Abale ndabwera ndinkhani yokwiyitsa.
Ndangomaliza kuyankhula ndi Mayi ku MILEPA kuja pa telephone.
Akuti mtumiki wina ataona kuti tinakapemphera nawo ,nayenso anapita(sizoletsedwa) koma chomvetsa Chisoni ndi choti anawakakamiza kuti ayime atamaliza mapemphero awo ,mpakana anawawongola mwendo ndikuthyoka ndipo ndikunena pano amayi aja ali mu ululu ndipo awaika chikhakha ndipo awagoneka ku Chipatala cha Chiradzulo.
Anthu a Mulungu anzanga, chonde mukapemphera ndi munthu , gwiritsani ntchito nzeru .Sibwino kumukakamiza munthu yemwe akudwala kuti achite zinthu zomwe sanachitepo nthawi yaitali. Nthawi zambiri thupi limakhala silinalandire mphamvu.
Mukawerenga mu Baibulo pa MACHITIDWE 3, munthu yemwe anali pa Kachisi uja anachita kumuthandizira kuti adzuke koma sanamukakamize kuti ayende.
Kupempherera anthu kumafunikanso chidziwitso ( knowledge of the word of God) komanso chikhulupiriro cha munthu mwini wake.
Sindikudziwa kuti anapita ndi ndani koma Ngati mukuwerenga Post iyi simunachite bwino kuwakakamiza kuti ayende. Nanga tamvani munthu wathyoka Bondo kamba kokakamizidwa ndi munthu wa Mulungu kuti ayime, thupi lawo linali lisanalimbe.
Pali machiritso ena amabwera pang'ono pang'ono ( Gradual Healing). Especially kwa omwe akhala akudwala nthawi yaitali.
Unfortunately amayiwo akuti sakumudziwa dzina lake mtumikiyu koma ananena kuti anawadziwa kudzera pa Facebook ,chifukwa choti tinapitako nkukapemphera nawo
Zandiwawa chifukwa amayiwa anachira kale titapemphera nawo muja ndipo amatha kukhala pansi bwinobwino.