26/07/2026
ACHINYAMATA A YOUNG AMO ACHITA NTCHITO ZA CHIFUNDO PA CHIPATALA CHACHING'ONO CHA NKHUNGA
Lero, pa 26 July 2026, achinyamata a gulu la Young AMO anachita pulogalamu ya Ntchito za Chifundo pa Chipatala Chaching'ono cha Nkhunga.
Monga mbali ya pulogalamuyi, achinyamatawa anakumana ndi amayi oyembekezera, kucheza nawo, kuwagawira mawu olimbikitsa ochokera m'Baibulo, komanso kuwaimbira nyimbo zotamanda Mulungu.
Elder Humphrey Kampira, omwe ndi sponsor wa gululi, ndi amene anawerenga Mawu a Mulungu kuchokera pa Genesis 22, pomwe Mulungu anayesa Abrahamu pomupempha kuti apereke mwana wake yekhayo, Isake, ngati nsembe. M'mawu awo analimbikitsa kuti ana onse ndi mphatso zochokera kwa Mulungu, choncho ayenera kuleredwa mogwirizana ndi chifuniro cha Mulungu. Anawerenganso Luka 2:52, ponena kuti amayi ndi aphunzitsi oyamba a ana awo, ndipo ali ndi udindo waukulu wowalera m'njira yoyenera.
Pambuyo pa uthengawo, achinyamatawa anapereka thandizo la zinthu zosiyanasiyana monga shuga, sopo, mafuta odzola, glycerin, ndi zinthu zina kwa amayi omwe anali pa chipatalapo.
Kenako anapitiriza ndi ntchito za ukhondo pa chipatalapo, kuphatikizapo kusesa bwalo, kufukura ngalande, kutchetcha udzu, komanso kukolopa malo osiyanasiyana.
Polankhula m'malo mwa mkulu wa chipatalacho, Mai Tembo, omwe ndi namwino, anayamikira kwambiri ntchito yomwe achinyamatawa anachita. Iwo anati:
"Mwapanga zinthu zazikulu kwambiri. Azimayi awa amasowa zinthu zambiri. Mwawapatsa uthenga wauzimu komanso katundu wothandiza. Mulungu akudalitseni kwambiri."
Nayenso mtsogoleri wa Young AMO, Success Heran, anasonyeza chisangalalo kuti cholinga cha gululi chikukwaniritsidwa. Iye ananena kuti achinyamata ali ndi udindo wotumikira Mulungu mwa kuthandiza anthu onse, mkati ndi kunja kwa mpingo. Anapemphanso utsogoleri wa mpingo kuti upitirize kuwathandiza ndi kuwathandizira pa mapulogalamu awo omwe akubwera.
Wolemba; Evangelist Humphrey Kampira