08/08/2025
Morning Devotion
Tayamba ndikupembezera, kupemphelera mabanja athu, mpingo wathu komaso chipembezo chathu chikubwelachi popeza chikutsogoleredwa ndi ana athu.
Tapempheleraso dziko lathu pamene tikuyembekezera ku voter nde taikiza mapemphero kuti Mulungu atithandizire kuti tisankhe mtsogoleri oopa Ambuye, Odziwa mau kuti dziko lathu lisapite kuchionongeko.
ULARIKI
tinawelenga ma bukhu awiri
2 Samueli 11:1
Ndipo kunali pofikanso chaka, nyengo yakutuluka mafumu, Davide anatumiza Yowabu, pamodzi ndi anyamata ake, ndi Aisraele onse; ndipo iwo anasakaza ana a Amoni, naumangira misasa yankhondo Raba. Koma Davide anatsalira ku Yerusalemu.
2 Samueli 11:2
Ndipo kunali pa madzulo Davide anauka pa k**a wake nayenda pa tsindwi la nyumba ya mfumu. Ndipo iye ali patsindwipo anaona mkazi alinkusamba; ndi mkaziyo anali wochititsa kaso pomuyang'ana.
2 Samueli 11:3
Ndipo Davide anatumiza munthu nafunsa za mkaziyo. Ndipo wina anati, Sindiye Bateseba, mwana wamkazi wa Eliyamu, mkazi wa Uriya Muhiti?
2 Samueli 11:4
Ndipo Davide anatumiza mithenga, namtenga iye; iye nabwera kwa iye, ndipo anagona naye, pakuti adachoka mumsambo; ndipo anabwereranso kunyumba yake.
2 Samueli 11:5
Ndipo mkaziyo anaima, natumiza munthu nauza Davide, kuti Ndili ndi pakati.
2 Samueli 11:6
Davide natumiza kwa Yowabu, nati, Unditumizire Uriya Muhiti. Ndipo Yowabu anatumiza Uriya kwa Davide.
2 Samueli 11:7
Ndipo pakufika kwa iye Uriya uja, Davide anamfunsa kuti, Yowabu ali bwanji? Ndi anthu ali bwanji? Ndi nkhondo ili bwanji?
Komaso
Tawelenga
Mateyu 12:43
Koma mzimu wonyansa, utatuluka mwa munthu, umapitirira malo opanda madzi kufunafuna mpumulo, osaupeza.
Mateyu 12:44
Pomwepo unena, Ndidzabwerera kunka kunyumba kwanga, konkuja ndinatulukako; ndipo pakufikako uipeza yopanda wokhalamo, yosesedwa ndi yokonzedwa.
Mateyu 12:45
Pomwepo upita, nutenga pamodzi ndi uwu mizimu ina inzake isanu ndi iwiri yoipa yoposa mwini yekhayo, ndipo ilowa, nikhalamo. Ndipo matsirizidwe ake a munthu uyo akhala oipa oposa mayambidwe ake. Kotero kudzakhalanso kwa obadwa oipa amakono.
Kumasulira
Mutu wa ulariki ndwo ULESI NDI TCHIMO
tikuona mfumu Davide anachita ulesi kupita ku nkhondo ndipo ulesi unabala tchimo losiona nkazi wa Uliya ulesi omwewo unamupasa chilakolako chogona naye ndipo atapereka mimba tikumuona akumuitanitsa Uliya kuti adzagone ndi nkazi wake kuti asadziwike kuti wapanga tchomo logona ndi nkazi wa mwini. Tikaipitiliza nkhaniyo ikulongosora kuti Uliya sanapite kunyumba kwake anagona ndi anyamata pa gate ya mfumu pachifukwa ichi mfumu Davide tikuiona ikumuledzeletsa Uliya ncholinga choti akagonebe kunyumba koma sizinatero pamapeto pake Davide wampanga chiwembu Uliya pouza wankulu wa nkhondo kuti amuike kutsogolo cholinga choti afe. Phunziro
Ukamulora Mulungu kuti akhale tate ndi mupulumitsi wa moyo wako ukhale omvera chomwe Mzimu oyera ukulamulira, chifukwa ukapanda kumvera Umakuchokera ukakuchokera chiwanda chimabwera ndi zinzake kulowa mwa iwe ndipo umakhala oyipitsitsa kuposa pachiyambi. Tikumuona Davide chifukwa cha ulesi wapanga tchimo losilira nkazi wa mwini , chifukwa cholipatsa mpata tchimo lakatenga machimo ochuluka kudzalowa mwa iye. Ndiko kusilira nkazi wamwini, kugona naye, kuledzeletsa Uliya, ndi kupha. Ambuye akudalitseni
Mkhale ndi tsiku lopambana
Amen.