Hpizzo.

Hpizzo. Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Hpizzo., nyirendahappy9@gmail. com, Blantyre.

Ndizotheka kuti pali anthu ena amene kanthuka sakadziwa. Pali nthawi zina zimene umatha kukhala ndi zinthu mu phone zomw...
28/05/2024

Ndizotheka kuti pali anthu ena amene kanthuka sakadziwa. Pali nthawi zina zimene umatha kukhala ndi zinthu mu phone zomwe ukufuna kupanga transfer kupititsa mu flash,

Ukakhala ndi kanthu aka sipafunikanso computer kuti transfer itheke. Umangokasomeka pamene pamalowa charger po basi...

Sikadula kanthu aka ayi.. ngati munthu amakwanitsa kupanga bundle, sungalephere kugula kameneka
Zikomo

Pano tikapeza ka bundle nkumaona zithunzi pa Facebook, chimwemwe chimabwela kutsayaku. Koma chimwemwe chimenechi siching...
24/05/2024

Pano tikapeza ka bundle nkumaona zithunzi pa Facebook, chimwemwe chimabwela kutsayaku. Koma chimwemwe chimenechi sichingapose chimene tinkamva tikaona galimoto ya a Fonta tikaweluka ku sukulu

Sukulu yomwe tinkaphunzira inali katali ndithu pafupi ma kilomita 5. Poweluka timakhala tatopelatu mudziwa mwana wa pulayimale okutinso anangolawira kusukusula nkumapita osakaona koti nkutafuna.

Sindikudziwa kuti ankakhala kuti akuchoka kuti, koma nthawi zambiri galimoto yawo simasowa munseu wa makata via Lunzu.

Tikaiona mitima yathu imadzala chimwemwe chifukwa timadziwa kuti lero mayendedwe akhala ophweka. Imangoima ife nkuthamanga kukakwela.

Timanyauda kwambiri maka tikakhala kuti tinaiputa nkhondo yoti poweluka tichotsane tonde mudziwa pachimwana, tikaiona galimoto ya a Fonta timadziwa kuti tapulumuka ku zibonyongo zimene wena anatikonzela kuti tikazinde kukakhala kwa mwai.

Sankapeza phindu lililonse kuchoka kwa ife, ngakhale ife nthawi imeneyo sitinkadziwa kuti akupanga chani. Kwathu kunali kunyauda kumva kukoma kuti takwela galimoto chimene chinali chapamwamba kwambiri.

Lero ndazindikira kuti chinali chufundo, ndi kukoma ntima. Analipo anthu amene ankangodutsa ndi magalimoto awo koma Iwo amakhuzika akationa tikuyenda pansi mtunda wautali.

Anali katswiri wapamwamba kwambiri. Mbili yake inamveka patali. Ana achichepele ngakhalenso achikulire amadziwa bwino za...
24/05/2024

Anali katswiri wapamwamba kwambiri. Mbili yake inamveka patali. Ana achichepele ngakhalenso achikulire amadziwa bwino za luso lake loomba Batcha mwaukadaulo. Dzina lake linali Dande.

Dande sanali oomba Batcha wawamba ayi chifukwa nyimbo ikafika pamtsetse amatha kusakaniza maombedwe a Batcha ndi chibwano, chitendene, chigonkono mwa Zina

Amathanso kuiomba Batcha ataisenza pa mutu ngakhale ataibeleka kunsana kwinaku ndodo zoimbira akumaziponya mmwamba ndikumaziwakha koma nyimbo osasokonekela.

Luso la nkuluyu linakopa anthu ochuluka ndipo anali kuitanidwa mu zochitika zosiyanasiyana monga mu zikwati, zinamwali, zinkhoswe, kulonga ufumu, misonkhano ya zipani ndi kulikonse kumene kungafunike mavume a Batcha.

Ndukumbuka mchaka china achibale ena anali ndi ukwati ku tawuni, ndipo ife tinayenela kukapezeka nawo kumeneko. Tinapita kukamusaka Dande kuti timvane kuti akhonza kufuna zingati kuti akativinise ku tawuni.

Tinayenela kunyamuka lachisano kuti tikachezele kujaza usiku onse chifukwa mwambo wa ukwati unali wa loweruka.

Galimoto linafika kudzatenga anthu a mmudzi kuti tikaiontse kutauni. Dande anachedwelapo kufika chifukwa amachokela mudzi wa patali. Nkhawa inathawa pamene tonse tidamuona wachikulire wa Batcha akutulukira ali wefuwefu.

Ulendo unayambika kupita ku taoni, nyimbo zoyeselera zikulikitika mu lole imene tinakwela kuti tikaone poyambira.

Mmene nthawi imati 6koloko madzulo nkuti tikufika mu tawuni ya BCA munzinda wa Blantyre. Tinalandilidwa bwino ndi chakudya muja mudziwira mwambo wa ukwati.

Dande anayenela kuchita zokonzekela pa ntchito yake monga kuwamba Batcha ndi Zina kuti nthawi iliyonse mchezo uyambe. Nawonso ma Dj aku tawoni, anali kugwiragwira zida zao za magetsi, kusonkhanitsa ma kaseti ndi Zina.

Nthawi imeneyo nyimbo zobheba zinali za achina Malume Bokosi, black missionaries kuimba3, Mwana mulamba, Dan K uja wa ku Zambia ndizina munthawiyo,Ndipo momwe kunakonzedwela mwambo unayambadi.

Kunali kusokonezana chifukwa Dj amati akafaka nyimbo yomwe yavuta nthawi imeneyo, ndipamene Dande naye akuonetsa zisuzo kubwalo lake lomwe anapatsidwa kuti onse okonda Batcha akakhaleko.

Anthu a kutawuni amati akabwera kuzasunzumira ku bwalo la mganda, samafuna kuchoka kamba ka dansi ya fumbi yomwe imatcholedwa kumeneko.

Zinafika pokuti mpaka choimba adazimitsa chifukwa chidwi Cha anthu tsopano chinali ku mganda umene Batcha yake imaimbidwa mopatsa chikoka.

Katswiriyu sanali kupambadza Ng'oma chabe, analinso ndi luso loimba nyimbo. Amati akaiyambitsa nyimbo anthu ovomeleza samasowa poigwira.

Zikafika pankomati Nchikulireyu amatha kutulusa voice ina yopatsa chidwi pena kumveka ngati akulira atayang'ana kumwamba kwinaku akupukusa mutu wake.

Ndikuti sanali munthu wamasewera ikafika nthawi yosangalatsa khamu.

M'mawa kutacha pa tsiku la mwambo wa ukwati anthu onse akutaoni anasonkhana kufuna kumuona Dande chifukwa usiku samamuona bwino amangomva ntchito za manja ake.

Komatu apa nkuti Wachikulireyo agona Kaye kuzitolera kukonzekela nkhondo yoomba Batcha pa mwambo weniweni masana ake. Komabe poti anali osazikweza, atadzutsidwa kuti kwabwera khamu la anthu amene amavina usiku uja, anadzuka kuti akumane nao.

Masana nthawi yoyamba mwambo inakwana, ndipo onse anakanisitsa kuvina nyimbo za pamagetsi. Katswiri Dande, anaigwira ntchito yotamandika mpaka mwambo onse wa ukwati unayenda mwa pamwamba zedi.

Anasiya mbiri yabwino ku tawuni
Legend Dande munthawi yathu.

12/05/2024

A message to the praise and worship teamw/ Caswel Mkanda

AKATSWIRI OJAMBULA NYIMBOKodi munayamba mwaganizapo za zomwe zimayenda mmutu mwa munthu amene anajambula nyimbo ija mmai...
09/05/2024

AKATSWIRI OJAMBULA NYIMBO

Kodi munayamba mwaganizapo za zomwe zimayenda mmutu mwa munthu amene anajambula nyimbo ija mmaikonda?

Musaiwale kuti kupatula mau amene amamveka mu nyimbo, pena mumamvekanso zing'wenyeng'wenye zomwe zimathandizilanso kuti nyimbo imveke mwapamwamba.

Dziwani kuti oimba nthawi zina amatha kupeka nyimbo, koma opanga ganizo lililonse la kamvekedwe ka zida. Amaipanga nyimbo momwe akufunira ndi momwe angakwanitsire muniwake.

Akafika mu studio, kwake kumakhala kumuimbira nyimbo ojambula. Nthawi zambiri maganizo a kamvekedwe ka zida, imakhala ntchito ya ojambula.

Si zida zokha, ngakhale nkhani ya mau, nthawi zina amatenga gawo lalikulu, kumuunikira muimbi kuti zimveke bwino.

Nyimbo iyambe bwanji kuti ikhale yopatsa chikoka? Nyimbo Zina maka za uzimu, kumakhala kukuwa ikamayamba, nthawi zambiri amakhala ma dongosolo a ojambula.

Oimba enanso zimatheka kulephera kukuwa
ikamayamba nyimbo. Kaya mmati chani chizungu chanucho ,koma mpaka ojambula ena amakhonza kuzipeleka ndikuikamo mau ao mu nyimbo pofuna kuti zimveke bwino, kapena kuthandiza kupeza munthu amene akhoza kuchita moyenera.

Tiyeni pomvera nyimbo zoimbidwa mwa luso, tizikumbukanso luso LA munthu amene analumikiza zonse kuti zimveke mokoma.

Siine oimba..koma okhuzika 😂

Address

Nyirendahappy9@gmail. Com
Blantyre

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Hpizzo. posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share