Evangelist Lennox Greman Mponda

Evangelist Lennox Greman Mponda Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Evangelist Lennox Greman Mponda, Off Limbe Machinjiri Road, Blantyre.

13/04/2025

YOHANE 6 V 55

Pakuti Thupi langa ndi chakudya ndithu ndi Mwazi wanga ndi chakumwa ndithu.

PHUNZIRO:

Yesu mmene ankayankhula izi ankadziwa kuti amene adye Thupi ndi kumwa Mwazi wake ndiye kuti akuyenera kukhala Munthu woyeretsedwa chifukwa mkate ukuimirira Thupi la Yesu ndipo Vinyo ukuimirira Mwazi wake wa Yesu Khristu.
Ndikudziwa kuti pali anthu ambiri amene adya Mkate komanso kumwa Vinyo koma ali opanga zinthu zosakhala bwino zimene zili zotsutsana ndi Malamulo a Yehova Mulungu wathu wa Moyo.
Dziwani kuti tisanadye Mkate komanso kumwa Vinyo timayenera kudziyeretsa polapa machimo athu ndipo tikadya ndi kumwa Thupi ndi Mwazi wake tikuyenera kukhala masiku Asanu ndi awiri tisanachite tchimo liri lonse. Apa Mau a Yehova amati; Musadye Mkate wotupitsa ayi. Ndipo dziwani kuti ngati tidya chotupitsa pang'ono ndiye kuti zonse zimene tichita ndiye kuti zisanduka zotupitsanso.
Chotupitsa pang'ono chitupitsa mtanda wonse. Apa tikuyenera kuchenjera pochita zinthu zathu osati tikondwe kuti tadya Thupi ndi kumwa Mwazi wa Yesu Khristu pamene mkati mwathu muli dumbo komanso milandu yambiri.
Ngati tachita zinthu zosakhala bwino tiyeni tigwade ndipo tilape chifukwa Mau a Yehova amati; Ngakhale tchimo litafiira ngati Kapezi koma tikalapa lidzayeretsedwa ngati Matalala.

Ambuye akudalitseni Abale ndi Alongo nonse.
Mukhale ndi Utsiku wabwino!

01/02/2025

MIYAMBO 7 Vs 1 - 3

Mwana wanga sunga mau anga, ukundike malangizo anga;
2 Sunga malangizo anga, nukhale ndi Moyo; Ndi malamulo anga ngati mwana wa diso lako.
3 Uwamange pa zala zako, Uwalembe pamtima pako;

PHUNZIRO:

Munthu akasunga Malamulo ndi Malangizo a Yehova Mulungu wathu wa Moyo amakhala ndi Moyo. Tiyeni tisunge Malamulo a Yehova ngati mmene timatetedzera mwana wa diso lathu kuwopa kuleka kuwona. Malamulo a Yehova tikuyenera kuwamanga pa zala zathu ndipo tiwamange pamitima yathu.
Ndikudziwa kuti pali anthu ena amene amawona ngati kunja kuno kulibe Mulungu koma dziwani kuti mukuchedwa kwambiri chifukwa tsiku lina mudzayankha zomwe mumachita pa dziko lino.
Kumbukirani kuti Yesu Khristu Mwana wa Yehova anabwera kudzakhala Munthu ku Thupi kuti amve zowawa komanso kufuna kupulumutsa Inu ndi ine.
Ndiye imfa ya Yesu tiyeni tiitenge kukhala yofunika kwambiri chifukwa kupyolera mwa imfa imeneyi ife tidzapedza Chipulumutso ngati tichita bwino.

Ambuye akudalitseni Abale ndi Alongo nonse ndipo mukhale ndi Tsiku Labwino.

31/10/2024

This podium is for you to spread the gospel and no one is prohibited to post here

22/02/2024

LUKA 12 V 35

Khalani odzimangira mchuuno, ndipo nyali zanu zikhale zoyaka.

PHUNZIRO:

Tikuyenera kuvala bwino titamanga Mabuluku athu ndi malamba olimba kupangira kuti pamene ntchito ya uthenga wa Mulungu wa Moyo ili mkati Mabuluku atha kutsika ndiye uthenga wa Mulungu udzasokonekera.
Mau akutinso: Nyali zanu zikhale zoyaka. Kutanthauza kuti Machitidwe athu akhale abwino osati Oipa ayi. Munthu amene wasankha kutumikira Mulungu akuyenera kukhala Woyera ndipo wipanda Banga.
Ngati tinachimwa ndipo tikuchimwabe tiyeni tirape Machimo athu kenako tiyambe kutumikira Mulungu Muuzimu ndi Mchoonadi.

Ambuye Yesu Khristu apitiridze kutiphunzitsa Mau amene tagawanawa kuti tsiku la Chiwerudzo nkudzapulumuka ndithu.

Tsiku labwino Abale ndi Alongo nonse

28/01/2024

1 SAMUEL 20 V 3

Ndipo Davide analumbiranso nati, Atate wako adziwa kuti wandikomera mtima; nati, Jonatani asadziwe ichi, kuti angamve chisoni; koma pali Yehova, ndiponso pali moyo wako, pakati pa ine ndi imfa pali ngati phazi limodzi.

PHUNZIRO:

Tamva mmene ndime 3 yafotokozera. Ndipo Anthu ambiri timadabwa Anthu akamatisiya nthawi zonse. Apa Jonatani akufotokoza bwino lomwe kuti; Pakati pa ine ndi imfa pali ngati phazi limodzi. Muyeso wa phazi suwaukuru kwa Mwini phazi ayi. Ngakhale utamavala size 15 koma kwa iwe phazi lako ndilaling'ono ndipo limawoneka larikuru kwa anthu ena.
Apa ndafuna kuti mudziwe kuti moyo tili nawo lerowu siwokhalitsa ayi.
Ndiye tiyeni tikafuna kuchita zinthu zathu tisakhale ngati ife ndi Amuyaya ayi. Tidziwe kuti ndife alendo pa dziko pano. Mulungu wathu wa Moyo anaikiratu nthawi yakubadwa ndipo nthawi yakumwalira akuidziwa.
Ngakhale timamwa Mowa kapena kutchuka ndi zibwenzi kapena kuthetsa mabanja a ena koma tonse tikudikira tsiku limodzi limene liri lakufa kwathu. Tiyeni tisamale Abale ndi Alongo.

TITANI KUTI TSIKU LA IMFA LISADZATIDZIDZIMUTSE:

Amene ayenda Mmau komanso Mchisomo cha Mulungu wathu wa Moyo ameneyo sakhala ndi mantha ndi imfa ayi. Tawona ena akufa atamva uthenga woti Mbale wawo wamwalira. Izi nzomvetsa Chisoni kwambiri.
Tiyeni tikonze njira yathu pomkakamira Yehova Mulungu wathu wa Moyo tsiku ndi tsiku ndipo tidzasimba lokoma Muufumu wa Mulungu.

Ambuye Yesu Khristu apitiridze kutiphunzitsa kuti likadzafika tsiku lathu lakufa tisadzakhale ndi nkhawa ayi.

Chisomo cha Mulungu wathu wa Moyo chikhale nanu nonse pamene mukukonzekera wa kumapemphero.

27/01/2024

Woipayo akapanda kuchita choipacho samagona turo!

18/01/2024

Welcome all to this page whereby we will be sharing the Almighty God's gospel in these last days

18/01/2024

Address

Off Limbe Machinjiri Road
Blantyre

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Evangelist Lennox Greman Mponda posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share