Word of God

Word of God Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Word of God, Blantyre.

19/09/2025

Ndikupemphera mu dzina la Yesu Khristu Mulungu akupambanitseni Mu Chilichonse, ndikusegula makomo achuma pa Moyo wanu mu dzina la Yesu Khristu Amen

18/09/2025

Opani Mulungu Ndipo musiyileni zosatira iye

03/09/2025

KULI NKHANI YANU KUNO

Aroma14:4
Salimo75:7
Mateyu7:1-7
1Petro2:23

Anthu ambiri,
mbili yawo inayipa
chifukwa okumvayo anamva mbali imodzi📌💔😣

Kuli anthu kunjaku akudutsa nyengo zowawa kamba koti owerudzawo anamva mbali imodzi😭

Ena anataya banja ndithu loti eni akewo ankakondana palibeso koma kamba koti ankhoswe anamva mbali imodzi
zinavutapo🙈

Ena munachosedwa ntchito kamba koti abwana anu anamva mbali imodzi💔

Munachosedwa sukulu kamba koti a head anamva mbali imodzi😢

Munachosedwa m'mpingo womwe mukaukonda kwambiri koma Abusa aja anamva mbali imodzi🤔

Munachoka dera lomwe munalikondesetsa kamba koti anthu akuderako anamva mbali imodzi🙄

Tamvetsera muwerudzi weniweni akadzaimilira panyengo zako udzaimba nyimbo ya chimwemwe ndipo misodzi yako ya chimwemwe idzaendelera ngati madzi osefukira kuli kusamvesetsa

Hallelujah 🙏

20/09/2022

SATANA MDIEREKEZI KWAKE NDI KUPHA, KUBA NDI KUONONGA. MWA IYE MULIBE CHOONADI, KUKHALA BWENZI LASATANA KUONONGA NTHAWI CHABE CHIFUKWA PALIBE CHABWINO CHOMWE MUNGACHIPEDZE MWA SATANA MDIEREKEZI.

LOLANI YESU KHRISTU ALAMULIRE MOYO WANU NDI KUTI IYE AKKHALE BWENZI LANU, NDIPO SIMUDZAKHUMUDWA ,IYE AZAKUPASANI MTENDERE NDI MOYO WOSATHA. MUKAKHULUPILIRA YESU KHRISTU KUKHALA MBUYE NDI MPULUMUTSI WA MOYO WANU, CHILICHONSE CHOMWE MUFUNA CHIDZAPASITDWA KWA INU.

(📖 11 🆚 28-30)
#28➡️Idzani kuno kwa ine nonse akulema ndi akuthodwa, ndipo ine ndidzakupumulitsani inu, senzani gori langa, ndipo phunzirani kwa ine: chifukwa ndiri wofatsa ndi wodzichepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. #30➡️Pakuti gori langa liri lofewa, ndi katundu wanga ali wopepuka.

-LA-KHRISTU

Okondedwa mwa Ambuye wathu Yesu khristu, Moyo ukuyenda bwanji kumene inu muli? Yesu khristu akuitana, bwerani kwa ine, bwerani kwa ine, musiyileni katundu wake satana. Ngati sakufuna kukutulani Ine Yesu khristu ndizakutulani.

Chifukwa alipo ena asing'anga anawapatsa chizimba koma anawauza kuti palibe kutembenuza, Tikunena pano atopa nacho chizimba koma pogwira alibe. Bwerani kwa Yesu khristu.

Alipo ena atopa ndikutumikira satanic koma akuopa athedwa nzeru chifukwa cha mantha. Moyo wawo uli pa chiopsezo chifukwa kusiya kwa satanic mkufa, Ai ai musaope, Bwerani kwa Yesu khristu ndamene ali ndi Mphamvu kuposa satana mdierekezi.

Kodi ndinu otchuka ndikutaya zimimba, mbava, wakupha, wabodza, wachiwerere, wolezera, wosuta fodya, Wochita machimo anyansisitsa
Bwerani kwa Yesu khristu, akufuna inu kuti akutuleni katundu wolemetsa wa satana mdierekezi.

Kodi inuyo mwatopa ndi chani? katundu wa machimo omwe inuyo mwanyamula mukuwadziwa. Yesu khristu akuti ngati mukufuna mtendere ndi moyo wosatha pa miyoyo yanu. Tipite kwa Iye sakusakha munthu, kapena kuchuluka kwa machimo akuti aliyense abwele kwa Iye.

Kuli bwino kusenza gori la Yesu khristu, kusiyana ndikusenza gori la satana. Chifukwa gori la khristu lili lofewa, Kwa bwino kuti anthu akunyozeni, akutukwaneni , anthu alakhule zoipa za inu, chifukwa cha Dzina la Yesu khristu.

Mukamatchuka ndi kukhwima, uhule, umbava, miseche, mabodza, kuba, kupha ndi ntchito zoipa zambiri zosiyana siyana. Wina akakunenani kuti wochimwa iwe mumapsa mtima chifukwa chani? Chifukwa kuti choti mumakhala kuti ntchito zoipa zimakusowesani mtendere chifukwa kuti inuyo mwasenza gori la satana.

Musaumitse mtima. Ali ndi Khutu amve, Amen

17/09/2022

MAKOLO NDI NTCHITO NDI UDINDO WANU KUWAWAPHUNZISA NDI KUWASOGOLERA ANA ANU KUYENDA NJIRA YA UMULUNGU.

(📖 22:6)
#6➡️Phunzitsa mwana poyamba njira yache: Ndipo ngakhale atakalamba sadzachokamo.

(📖 LUKA 18🆚15-16)
#15➡️Ndipo anadza nawo kwa iye ana amakanda kuti awakhudze; koma pamene ophunzira anaona, anawadzudzula. #16➡️Koma yesu anawayitana, nanena, lolani ana adze kwa ine, ndipo musawaletse; pakuti ufumu wa Mulungu uli wa otere.

(📖 29:17)
#17➡️Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa; Nadzasangalatsa moyo wako.

(📖 5:19)
#19➡️Pamenepo Yesu anayakha kwa iwo nati, indetu, indetu, ndinena kwa inu, sakhodza mwana kuchita kanthu payekha, koma chimene anaona atate achichita, ndicho. Pakuti zimene iye azichita, zomwezo Mwananso azichita momwemo.

(📖 4🆚39-40)
#39➡️Potero dziwani lero lino nimukumbukire m'mitima mwanu, kuti Yehova ndiye Mulungu, m'thambo la kumwamba ndi pa dziko lapansi; palibe wina. #40➡️Muzisunga malemba ache, ndi malamulo ache, amene ndikukuzani lero lino, kuti chikukomereni inu ndi ana anu akukutsatani,
ndi kuti masiku anu achuruke pa dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu kosatha.

(📖 20:7)
#7➡️ Wolungama woyenda mwangwiro, Anache adala pambuyo pache

(?? 6:4)
#4➡️Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi chilangizo cha Ambuye.

(📖 11:19)
#19➡️Ndipo muziwaphunzitsa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala inu pansi m'nyumba mwanu, ndi potenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pakuuka inu pomwe.

(📖 22:15)
#15➡️Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana; koma ntyole yomlangira idzauingitsira kutari.

(📖 17:10)
#10➡️Chidzudzulo chilowa m'kwati mwa wozindikira, kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

(📖 33🆚8-9)
#8➡️Ndikati ine kwa woipa, woipawe, udzafa ndithu, osanena iwe kumchenjeza woipayo aleke njira yache, woipa uyo adzafa m'phulupulu yache, Koma mwazi wache ndidzaufunsa pa dzanja lako. #9➡️Koma ukachenjeza woipa za njira yache, aileke; koma iye osaileka njira yache , adzafa m'mphulupulu mwache iye, koma
iwe walanditsa moyo wako.

(📖 22:19)
#19➡️Ndipo ali yense akachotsako pa mau a buku la chinenero ichi, Mulungu adzamchotsera gawo lache pa mtego wa moyo, ndi mzinda woyerawo, ndi pa izi zilembedwa m'bukumu.

Makolo phunzitsani ana anu za uthenga wa bwino wa Ambuye wathu Yesu khristu, tiwalondolere njira yachipulumutso kuti asatayike. Ambuye Yesu akudalitseni.

07/09/2022

"NTCHITO ZA SATANA MDIEREKEZI MUSAMAZIPHWEKETSE KAPENA KUZIDELERA, ZIMAONONGA, ZIMASOKELETSA, ZIMAZUNZA NDIPO ZIMAPHA. ANTHU AMBIRI AKUVUTIKA KWAMBIRI LERO CHIFUKWA CHOCHITA UCHIMO.

MOYO WA MUNTHU UMAFUNIKA AMBUYE YESU KHRISTU BASI, YESU KHRISTU NTCHITO ZAKE SIZIZUNZA ZIMAPATSA MTENDELE WOSATHA.

(📖 1 11 🆚 1_13)

(📖 8:44)
#44➡️ Inu muli ochokera mwa atate wanu mdierekezi , ndipo zolakalaka zache za atate wanu mufuna kuchita. Iyeyu anali wambanda kuyambira pachiyambi, ndipo sanaima m'choonadi, Pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene alankhula bodza, alankhula za mwini wache; pakuti ali wabodza, ndi atate wache wa bodza.

(📖 3:13)
#13➡️Ndipo Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, chiyani chimene wachitachi? Ndipo anati mkaziyo, Njokayo inandinyenga ine, ndipo ndinadya.

(📖 12:12)
#12➡️ Chifukwa chake, kondwerani, Miyamba inu, ndi inu akukhala momwemo. tsoka mtunda ndi nyanja, chifukwa mdierekezi watsikira kwa inu,Wokhala nawo udani waukuru, podziwa kuti kamtsalira kanthawi.

(📖 12:9)
#9➡️ Ndipo chinaponyedwa pansi chinjoka chachikulu, njoka yokalambayo, iye wotchedwa mdierekezi ndi satana, wonyenga wa dziko lonse ; chinaponyedwa pansi kudziko, ndi angelo ache anaponyedwa naye pamodzi.

Satana mdierekezi alibe mantha ndi mmene Mulungu wakhala akukugwilitsira ntchito, iye amayesesabe kupeza njira yakuti athane nawe. Ichi ndi chifukwa chake anthu amphamvu, azitumumiki, azibusa ndi anthu otchuka amatha kutayika ngati sasamala ndi kudalira pa Yesu khristu.

Pajatu satana mdierekezi, Yesu weni weniwo mwini Moyo ndi zolengedwa zonse, anamuyetsa kuti amugwetse koma analephera chifukwa Yesu anaima pa Mau ndi chikhulupiliro mpaka satana anagonjetsedwa.

Chimodzi modzi inu ndine tikuyenera kuima pa Mau a Mulungu ndi chikhulupiliro tidalire Yesu khristu akhale Ambuye ndi mpulumutsi pa miyoyo yathu, kuunika pa Miyoyo yathu kuti oipayo akabwera ndi machenjelero ake , mabodza ake timugonjetse. Ali ndi Khutu amve, Amen.

31/08/2022

~NAWO~ADANI~ATHU~TISABWENZERE~CHOIPA~CHILICHONSE.

(📖?? 4🆚17_32)
26➡️Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire.

(??🙏 15:17)
17➡️ Zinthu izi ndilamulira inu, kuti mukondane wina ndi mnzache.

(??🙏 15🆚12_14)
12➡️Lamulo langa ndi ili, kuti mukondane wina ndi mnzache, monga ndakonda inu. 13➡️ Palibe munthu ali nacho chikondi choposa ichi, chakuti munthu ataya moyo wache chifukwa cha abwenzi ache. 14➡️Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulirani inu.

(📖?? 13🆚34_35)
34➡️ Ndikupatsani inu lamulo latsopano, kuti mukondane wina ndi mnzache, monga ndakonda inu, kuti inunso mukondane wina ndi mzache . 35➡️Mwa ichi adzazindikira onse kuti muli akuphunzira anga, ngati muli nacho chikondano wina ndi mnzache.

(??🙏 6🆚 20_49)
35➡️Koma takondanani nawo adani anu, ndi kuwachitira zabwino, ndipo kongoletsani osayembekeza kanthu konse, ndipo mphotho yanu idzakhala yaikulu, ndipo inu mudzakhala ana a wamkurukuruyo: chifukwa iye acitira zokoma anthu osayamika ndi oipa. 36➡️Khalani inu achifundo monga atate wanu ali wachifundo. Ndipo musamaweruza, Ndipo simudzaweruzidwa.

(📖🙏 6🆚27_28)
27➡️Koma ndinena kwa inu akumva, kondanani nawo adani anu; chitirani zabwino iwo akuda inu. 28➡️Dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akuchitira inu chipongwe.

(📖🙏 5🆚17_48)
44➡️Koma ine ndinena kwa inu, kondanani nawo adani anu, ndi kupempherera iwo akunzuza inu.

▶️Tikuzitchula tokha akhristu, maudani ali bweee ndi anthu. Osafuna kuti tithese maudani athu ndi anthu ena. Ukhristu onama umenewo, tipite tikayanjane ndi adani athu kuti kupembedza kwathu kukhale koona pamaso pa Mulungu.
▶️Azibusa, azitumiki, akulu ampingo maudani ali bweee mumpingo ndi akhristu anu , zaka kumatha, mukupemphera pachabe osafuna kukhululukirana ndi kuyanjanaso ndi amangawa anu ,ukhristu wa wokhotakhota.

➡️Tikhala bwanji akuphunzira ake a Yesu khristu ngati tilibe chikondi ndi anzathu.
➡️Tikhala bwanji akuphunzira ake a Yesu khristu ngati Sitifuna kukhululukira adani athu, Tikhala bwanji omusatira Yesu ngati sitikufuna kuyanjana ndi adani athu.

▶️Anzathu akuvutika ife tili nazo zinthu zoti titha kuwathandizira koma tangoziumilira, Tidziwe kuti ngati tili chonchi mwa ife mulibe choonadi, ngati tili chonchi tilibe chikondi, chikhristu chathu chopanda phindu kotheraku.

Ngati tifuna kusatira YESU khristu choyamba tikhale ndi chikondi pawina aliyense, amene ali ndi khutu amve, Ndikudandaulirani.

31/08/2022

ZATHU_ZOIPA_TITEMBENUKE_MTIMA.

(📖 6 🆚 16_19)
#16 Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi Mulungu azida; Ngakhale Zisanu ndi ziwiri zimnyansa: #17 Maso akunyada, lilime lonama, Ndi manja akupha anthu osachimwa; #18 Mtima woganizira ziwembu zoipa, Mapazi akuthamangira mphulupulu mmangu mmangu; #19 Mboni yonama yonong'ona mabodza, Ndi wopikisanitsa abale.

(📖 19 🆚 9)
#9 Mboni yonama sidzapulumuka chilango, Wolankhula mabodza adzaonongeka.

(📖 16🆚5)
#5 Yense wonyada mtima anyansa Yehova; Zoonadi sadzapulumuka chilango.

(📖 32 🆚 41)
#41 Ndikanola lupanga langa lonyezimira, Ndi dzanja langa likagwira chiweruzo; Ndidzabwezera chilango ondiukira, Ndi kulanga ondida.

(?? 23 🆚 33)
#33 Njoka inu, obadwa inu a mamba, mudzatha
bwanji kuthawa kulanga kwache kwa gahena?

(📖 2 1 🆚 8 )
#8 M'lawi lamoto, ndi kubwezera chilango kwa iwo osamdziwa Mulungu,Ndi iwo osamvera uthenga wabwino wa Ambuye wathu yesu.

(📖 13 🆚 4)
# Pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu, kuchitira iwe zabwino. Koma ngati uchita choipa opatu, pakuti iye sagwira lupanga kwachabe; pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu wakukwiyira ndi kubwezera chilango wochita zoipa.

▶️Tchimo pano anthu ayesa choseweretsa, Tchimo pano anthu ayesa bwenzi lawo, Tchimo pano anthu ayesa thandizo lawo, Zoti tchimo ndiloipa anthu sakutekeseka kapena kugwedezeka kapena kuopa, anthu amanga madziko patchimo.
▶️Zoti Mulungu amadana ndi tchimo, anthu alibe nazo ntchito, anthu akudana ndi Mulungu, anthu akudana ndi kumva zauthenga wabwino, pano anthu mitima mwawo mwazala ndi kuchita zoipa, Uthenga wa Mulungu ndichipsinjo pa moyo wawo.

▶️Satana ndi ziwanda zake apanga zinthu zambiri zokomedwetsa , zokongokola zimene anthu poziona akuziona ngati ndi zabwino koma mathero ake ndi opweteka kwambiri mosaneneka.
▶️Satana moyo wa Munthu alibe nawo ntchito, yeyo akungofuna kutiononga basi, kutilekanitsa ndi Mulungu, kuti Munthu alephele kukalowa ufumu wakumwamba, chimenecho cholinga cheni cheni cha satana.

Mulungu akutichenjeza ndi kutiululira zinsinsi za zinthu zomwe iye azida ndi zomwe iye zimanyansa, Chifukwa iye ndi Mulungu wachikondi ndi Mulungu wachifundo.

Ndikudandaulirani okondwedwa mwa Ambuye wathu Yesu khristu, Fewetsani mitima yanu ndi kutembenuka mtima , kuti Mulungu asanagwile lupanga lake lonyezimira ndi kutilanga atipeze titakonza moyo wathu. Ntchito zathu zoipa titasiya kuti kwa ife kukhale bwino. Amen.

29/08/2022



(📖🙏 6 vs 1_4)
#1 Yang'anirani kuti musachite zolungama zanu pamaso pa anthu kuti muonekere kwa Iwo; Pakuti ngati mutero mulibe mphotho ndi atate wanu wa kumwamba. #2 Chifukwa chache pamene pali ponse upatsa mphatso za chifundo, usamaomba lipenga patsogolo pako, monga amachita onyenga m'masunagoge, ndi m'makwalala, kotero kuti atamandidwe ndi anthu. Indetu indetu ndinena kwa inu, iwo alandiriratu mphotho zawo. #3 Koma iwe popatsa mphatso dzanja lako lamanzere lisadziwe chimene lichita dzanja lako lamanja; #4 Kotero kuti mphatso zako zachifundo zikhale zam'tseri; ndipo atate wako wakuona zam'tseri adzakubwezera iwe.

▶️Tisamale ndi kusata malamulo Pamene tikupeleka zachifundo kapena kuthandiza ena munjira zosiyana siyana, kuti kupeleka kwathu kukhale kolungama ndi kokondweletsa Mulungu.

▶️kupeleka kwathu kapena kuthandiza kwathu kukhale kwa chinsinsi kapena kobisa, tisamuthandizile munthu pa gulu pa anthu kuti anthu atitamande kapena atiyamikile chifukwa choti tathandiza .

▶️Tikamuthandiza m'zathu osowa, ovutika kapena kupeleka za chifundo, tisawakumbe kapena kulengezetsa kwa anthu ena , kuima pa chulu kuti anthu adziwe kuti mwathandiza.

▶️Tisapange za chifundo kapena kuthandiza osowa pamaso pa anthu, ngati mene anthu wonyengawo amachitira. amafuna kuti anthu atamande, apope, akonde. Chifukwa cha kupeleka kwawo kwa bodza ndi kwa chinyengo, pamaso pa Mulungu palibe mphotho imene amapeza chifukwa amakhala kuti zawo alandiliratu.

▶️Pothandiza ena anthu asadziwe, mupite mwa
m'tseri mosaonetsera kuti kuthandiza kwanu kuwelengedwe pa maso pa Mulungu, kuti iye mwini akupaseni mphotho yanu, kuthandiza kwanu kukhale kodziwana inu ndi Mulungu wanu.

▶️Mulungu amaona chilichonse cha m'tseri maso ake si akhungu, khutu lake limamva chilichonse ndipo silogotha, ndipo Mulungu amadziwa chilichonse ngakhale chisanachitike. Kuthandiza kwanu mwa m'tseri sikuti mumakhala mwabesa kapena kuti palibe chomwe mwachita ayi, koma iye mwini amakhala kuti ali ndi mphotho yaikulu yopotsa kutamandidwa ndi anthu a dziko lapansi.

▶️ Mulungu amadana ndi anthu osamvera amene amalephera kusatira malamulo ake , Wodzikweza amamutsisa, wodzichepetsa amamukweza.

▶️Iye ndiye Yehova Mulungu wachilungamo, Mulungu wachikondi, Mulungu wachifundo amene samalanga munthu asanamuchenjeze.

Ambuye wathu Yesu khristu atithandize ndi kukhala nafe, ndi kulakhula ndi miyoyo yathu. Pamodzi ndi mzimu woyera, Amen.

26/08/2022

?

Mulungu
Pamene tachimwa ubale wathu ndi Mulungu umakhala waduka ndipo sipamakhalanso kulumikizana.


Ukachimwa okondedwa kumakhala kuzunzika, mwina nkufunsa kuti motani?
✍️Tchimo lachigolo limabweretsa chizunzo pa matenda monga; HIV Ndi matenda ena ambiri osiyana osiyana.
✍️Tchimo lakuba limabweretsa chizunzo monga; kukhapidwa, kumangidwa, udani ngakhalenso imfa kumene.


Munthu ukachimwa, chikumbumtima chimakugwira ndipo umayamba kulingalira za choipa chomwe wachitacho. Mwachitsanzo, ukamachita tchimo lachigololo. Umakhala ndi nkhawa yoti koma akazanga/amunanga atangodziwa zindithera bwanji.


Monga baibulo limafotokonzera kuti mphoto yake uchimo ndiye imfa. Kusonyeza kuti machimowa tikamachita, tidzindikilenso kuti imfa ingathe kubwera Pakati pathu. Mwachitsanzo; Tchimo lokuba anthu akakugwila ukuba amatha kukupha pompo mpopo chifukwa cha tchimo lokuba. Tchimo la chigololo, anthu akumatenga matenda osiyana siyana gwero lake ndi imfa.( :23📖🙏)Pakuti mphoto yache ya uchimo ndi imfa; koma mphatso yaulele ya Mulungu ndiyo moyo wosatha wa mwa Yesu khristu ambuye wathu.
( :36📖🙏)Koma wondichimwira apweteka moyo wache; Onse okundida ine akonda imfa.( :15📖🙏)


Popeza tikachimwa Mulungu amatichokera , zikutathaunzaso kuti mzimu woyera otisogolera kuchita zabwino umatichokeranso. Izi zikutathaunza kuti mzimu woyera ukachoka pa moyo wathu sitingathe kudziletsa pamene tikuchita zoipa. Munthu akayamba kuchita tchimo mwai oziletsa kupanga zoipa umakhala wochepa chifukwa amakhala kuti mwa iye mulibe mzimu woyera.


( :12📖🙏) Pakuti maso a Ambuye ali pa olungama, Ndi makutu ache akumva pembedzo lawo; Koma nkhope ya Ambuye iri pa ochita zoipa.

Tilipo ambiri tidayamba kupempha kale kale, ambuye ndipatseni ntchito, banja,ana, chuma, bussiness, koma palibe yankho pa zopempha zanu. Zifufuzeni, ziunguzeni nkutheka kuti mudachimwa ndipo simunalape zapangitsa kuti Mulungu asakuyakheni zopepha zanu.

Okondedwa tchimo ndi loopsa kwambiri!!! ndipo limatilepheretsa zambiri. Talapani lero kwa Ambuye wathu Yesu khristu, akukhululukirani popeza iye adati gogodani chitseko chidzasekulidwa kwa inu. Mulungu akudaliseni pamene mwapanga chitsankho cholekana ndi tchimo. AMEN

Address

Blantyre

Telephone

+265883295542

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Word of God posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Word of God:

Share