Pastor Fredrick Mponda

Pastor Fredrick Mponda Glory to God

Choonadi chimamasula Pali anthu ochuluka omwe pano ali mumapiri, kusala kudya kupempherela zithu k*ti zitheke, koma vuto...
30/05/2026

Choonadi chimamasula

Pali anthu ochuluka omwe pano ali mumapiri, kusala kudya kupempherela zithu k*ti zitheke, koma vuto lalikulu lomwe ali nawo ndi khalidwe

Wokondedwa Pali anthu omwe a kupemphera kufuna mabanja koma sik*ti mwayi wa Banja alibe aii Ndithu koma vuto ndichikhalidwe

Alipo wina Ndithu pansi pa mtima amadziwa ndithu k*ti Banja likumuvuta chifukwa ca umbombo, wina alipo ndithu pansi pa mtima akudziwa k*t uhule, ndewu, mwano ndi zomwe zikupangitsa k*ti Banja lizindivuta,

Kudziwa vuto lako ndi bwino kusiyana ndikusitha mipingo, atumiki

Ena alipo sali pa ntchito vuto sik*ti mwayi wa ntchito alibe koma chikhalidwe, kupita ku ntchito atalezera, Kuba, izi ndi zithu zomwe ena zikuwapangitsa kukhala malova

Wokondedwa ndi bwino kumupempha Mulungu k*ti akonze makhalidwe athu oipa amene akubweretsa mavuto pa m'moyo yathu

Osamangoti satana, amfiti anandiloza ine, tikuziloza tokha chifukwa ca makhalidwe athu oipa,

Glory be to God all the time

Mulungu atamudalitsa Yosefe kufikira kukhala wolamulira dziko la Aigupto, sanasungire mkwiyo kapena udani kwa abale ake ...
29/05/2026

Mulungu atamudalitsa Yosefe kufikira kukhala wolamulira dziko la Aigupto, sanasungire mkwiyo kapena udani kwa abale ake omwe anamugulitsa

Genesis 45:4,Ndipo Yosefe anati kwa abale ace, muyandikiretu kwa ine, nayandikira, ndipo iye anati, ine ndine Yosefe m'bale, ine ndemwe munandigulitsa ndilowe m'Aigupto,. 5 Tsopano musaphwetekwe mtima, musadzikwiyira inu nokha, k*ti munandigulitsira ine kuno, Pak*ti Mulungu ananditumiza ine pa tsogolo panu k*ti ndisunge moyo.

Wokondedwa tamumveni Yosefe mmene akuwayankhulira abale ake amene anamugulitsa, koma iye anawayankhula mwachikondi mosawelengera za zomwe anamuchitira

Yosefe anaona k*ti anali Mulungu yemwe analora k*ti iye apite ku Aigupto ndi cholinga choti azasunge moyo wa abale ake, wokondedwa pamene Mulungu watidalitsa kapena kusitha mbiri yathu, tisamawakhwiyire kapena kuwada anthu omwe anatidzudza

Ndik*theka Pali munthu wina wake yemwe anakudzudzana inu muli wang'ono, kapena zanu zisanayende koma pamene Mulungu akukudalitsani mutsasungire mangawa

Pali anthu ena amafika pomati Mulungu akazandidalitsa amene aja azandimva, wokondedwa Ndik*theka munachitidwe zowawa ndi munthu yemwe mukakhala Naye, amakudzudzani, koma khululukani pachina chilichonse chomwe anakuchitirani ndi kuchotsa mangawa mumtima mwanu

Mulungu akudalitseni

18/05/2026

Luka 5:4 ndipo pamene iye analeka kulankhula anati kwa simoni kankhira kwakuya nimuponye makoka 6ndipo pamene anachita ichi anazinga unyinji waukulu wamsomba.Okondedwa nk*theka tikupemphela koma mayankho sakupezeka tiyeni tipemphele mwakuya pena pena kusala kudya pena kukwela phiri pena pena kuwinda anthufe mapempheledwe sangafanane,ziwani k*ti nkhondo zathu sizofanana amen

Zochepa zomwe muli nazo ndi bwino kumamuyamikira Yehova, ena akuvutikira k*ti azipezo zomwezo, anthu ena akusalira kudya...
02/05/2026

Zochepa zomwe muli nazo ndi bwino kumamuyamikira Yehova, ena akuvutikira k*ti azipezo zomwezo, anthu ena akusalira kudya, kukwera mapiri k*ti ape zomwe inu muli nazo

Wokondedwa ndi bwino nthaw zonse tikhale anthu woyamika, zochepa zomwe tili nazozi ndi bwino Ndithu tizinena zikomo Yehova, Kuja kuno anthu akuvutika

Glory be to God all the time

Mulungu alibe size Yake, akafuna kumanga nyumba yako ngakhale adani ako amathandizira kuperekera matopeAmene amati sizng...
01/05/2026

Mulungu alibe size Yake, akafuna kumanga nyumba yako ngakhale adani ako amathandizira kuperekera matope

Amene amati sizngatheke, sungakwanitse, amene anatemberera tsogolo lako k*ti osazapite chitsogolo, usadzakhale pa Banja, usadzapeze ntchito, uzingodwaladwala akhale woyanba kuchitira umboni za zimene Mulungu akuchita pa iwe mwezi uno

Estere 6:10 Pamenepo mfumu inati kwa Hamani fulumira, tenga cobvala ndi kavalo monga umo wanenera, nucitire cotero Moredakai Myudayo wokhala pa cipata ca mfumu, kasasowepo kanthu ka zonse wazinena

Halleyu!!!

Umachokera ku Banja lovutika, kulibe munthu woti angak*thandize koma sumaziyang'anira pansi umayetsayetsa k*thamangatham...
28/04/2026

Umachokera ku Banja lovutika, kulibe munthu woti angak*thandize koma sumaziyang'anira pansi umayetsayetsa k*thamangathamanga ndi mtima woti Siku lina uzakhale iwe uthandiza abale ako, Mulungu ak*tsegulire makomo azachuma amene wakhala uku gogoda kwa zaka zaka... Mu dzina la Yesu khristu Amen

Wina wake, kwina kwake asowe mtendere kufikira k*ti akukumbukire iweyo, Onse amene anakuyiwala ayambe kukumbukira iweyo ...
25/04/2026

Wina wake, kwina kwake asowe mtendere kufikira k*ti akukumbukire iweyo, Onse amene anakuyiwala ayambe kukumbukira iweyo Kaya Pali mwayi wa ntchito penapake dzina lako likhale loyamba kukumbukiridwa

Estere 6:1, Usiku uja tulo tidamwazikira mfumu niti, abwere nalo buku la mbiri, naliwerenga pamaso pa mfumu. 2,Napeza mudalembedwa k*ti Moredekai adaulula za Bigitana ndi Teresi awiri a dindo a mfumu osunga pa khomo, amene adayesa kumthira manja mfumu Ahaswero. 3,Niti mfumu, anamcitira Moredekai ulemu ndi ukulu wotan chifukwa ca ici? A nanena nayo sanamcitire kanthu.

Halleyu!!! Wokondedwa mwa Ambuye, Ndik*theka wakhala ukuponderezedwa pa ntchito, nthaw yako yakwana yoti ulandira Promotion, nthaw yako yakwana k*ti anthu omwe anakuyiwala ayambe kukumbukira chifukwa Yehova wagwira file yako

Nthaw yako yakwana naweso uchitire umboni, wakhala munthu woombera manja ma umboni a anthu ena, wakhala omvera ma umboni a anthu ena nthaw yako yakwana ena amvere wako

Nthaw yoti kumwamba kukuchitire kathu pa mapemphero ako aja yakwana, nsembe zako zija, zowinda zako zija, za chifundo zako zija yakwana

Amene wanyamula chosowa chako asowa mtendere kwina kuli konse komwe ali mu dzina la Yesu khristu Amen

Osafooka, Osatopa ndi kukhala wokhulupilika pa maso pa Mulungu, Mulungu amapereka mphotho

Glory be to God all the time!!!!

Nkhawa za moyo wathu Luka 12:25,Ndipo ndan wa inu, ndi kuda nkhawa angathe kuonjeza mkono pa msinkhu wace? 26 kotero nga...
23/04/2026

Nkhawa za moyo wathu

Luka 12:25,Ndipo ndan wa inu, ndi kuda nkhawa angathe kuonjeza mkono pa msinkhu wace? 26 kotero ngati simungathe ngakhale cacing'onong'ono muderanji nkhawa chifukwa ca Zina zija?

Wokondedwa nkhawa ndi matenda owopsa, tiyeni tipewa kukhala mu nkhawa pokhala anthu wosangalala nthaw zonse

Ndi nyengo yanji kapena nkhan yanji yomwe ikubweretsa nkhawa pa moyo wanu, ndi kusowa zovala kod? Chakudya kapena? Kapena nkhan za ku ntchito? Kapena za banja lanu, kapena nthazi lanu,

Nkhawa zanu zonse mutulireni Yehova ndi amene ali ndi ma yankho ankhawa zanu zonse , monga iye ali landlord wa moyo uno, musazikakamire nokha simuzitha

Yesu ndiye bwezi lodalilika, limene ukaliuza za mavuto ako silik*tseka kapena kungokhala chete ndi bwezi lomwe limabweretsa yankho pa mavuto ako

Ophunzira atamudzutsa Yesu pa nyanja, pamene panauka namodwe sanakhale chete anadzuka ndikulamula namodwe k*ti akhale abata, ali yemweyo kudzuka pa nyengo zako angodikira iwe umuuze, k*ti Ambuye loweleranipo pa nyengo zangazi

Palibe yemwe anadikira pa Mulungu ndi kuchita manyazi

Osamakhala ndi nkhawa, stress free in Jesus name Amen

Always be Happy, remember Happiness is free no need to be rich to be happy

Kudziwa mphatso yakoKodi mumadziwa mphatso imene Mulungu anakupatsani? wokondedwa ndi bwino k*ti munthu azidziwa mphatso...
20/04/2026

Kudziwa mphatso yako

Kodi mumadziwa mphatso imene Mulungu anakupatsani?

wokondedwa ndi bwino k*ti munthu azidziwa mphatso yake

1 Akolinto 12:7, Koma kwa yense kwapatsidwa maonekedwa a mzimu k*t apindule nao,

Ndibwino kumasamalira mphatso imene Mulungu anatipatsa ndi kuyigwilitsa ntchito chifukwa ndiyomwe ipindulitse moyo wathu

Mphatso ndi luso muli nalo zigwiritseni ntchito, Kaya ndi inu woyimba imbani Ndithu, Kaya nd inu osewera mpira sawelani Ndithu, Kaya mphatso yanu ndiyochita business pangani ndithu, Kaya luso lililonse ligwiritseni ntchito ndithu

Pamene Munthu sukudzidziwa chimene uli, umakhala moyo wa try and error, zaka ndikumapita, musayipeputse mphatso yanu igwiritse ntchito ndithu, Kaya nd ya utumiki, tumikirani ndithu

Ndipemphero langa kwa munthu wina aliyense amene ali kulingalira kapena kufunafuna atadzidziwa chimene akuyeneka k*ti azichita kapena akhale Mulungu akudzindikiritseni mu dzina la Yesu khristu Amen

OPERATION BWEZANMngelo yemwe ananyamula uthenga wa Danieli anagwidwa ndi mafumu a Perisiya kwa masiku makumi awiri ndi l...
17/04/2026

OPERATION BWEZAN

Mngelo yemwe ananyamula uthenga wa Danieli anagwidwa ndi mafumu a Perisiya kwa masiku makumi awiri ndi limodzi, ndipo taonani Mikaeli wina wa akalonga omveka, anadza kundithandiza, Danieli 10 :13,

Mulungu akuchotseni mphamvu iliyonse yakumidima imene yakhala ikuchedwa zithu pa moyo wako, madalitso ako

Pena zithu kumakhala ngati zikufuna ziyenda, koma from nowhere zithu kungowona zasokonekera Mulungu akuchotse mu mziwu uwu

Mulungu akumenyere nkhondo ku mphamvu iliyonse yakumidima imene inagwira ma yankho ako, kufikira k*ti zomwe wakhala ukupempherela uzilandire mu dzina la Yesu khristu Amen

Operation bwezani Yemwe anaba m'dalitso wako, anagwira ma yankho ako awalavure moto wa Yehova

Glory be to God all the time

Yosefe sanakhale mkaidi masiku onse amoyo wake, inakwana nthaw anakhala fulu ndikumathandiza abale akeYobu sanakhale mu ...
15/04/2026

Yosefe sanakhale mkaidi masiku onse amoyo wake, inakwana nthaw anakhala fulu ndikumathandiza abale ake

Yobu sanakhale mu ukapolo moyo wake onse, inakwana nthaw Mulungu anamuchotsera ukapolo wake

Yobu 42:10 Ndipo Yehova, anachotsa ukapolo wa Yobu,..... Yehova ameneyu akuchotsere nyengo ya ukapolo yomwe ili pa moyo wako

Kumanda kulibe kuchitira umboni, ulandira zosowa zako uli ndi moyo choncho k*ti umboni wako ulimbikitse nawo anthu ena

Osachoka pamaso pa Mulungu ndikirabe ngakhale zikuwawa, palibe yemwe anadikira pa Mulungu ndi kuchita manyazi

Tsiku lina ukhale iwe ukuperekera umboni, Mulungu at abwezeretsa zomwe unataya, atasitha mbiri yako from Nobody to Somebody, atachilitsa nthenda zako

Wosataya mtima, your time is coming

Address

Blantyre

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Pastor Fredrick Mponda posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share