13/05/2026
*TIYANKHULENI AMBUYE*
*13 MAY, 2026*
*LACHITATU LA MULUNGU WA 6 WA PASAKA*
*MAU A MBUKU LA NTCHITO ZA ATUMWI 17:15,22-18:1*
Anthu, amene adaperekeza Paulo aja, adakafika naye mpaka ku Atene. Pambuyo pake adabwerera ku Bereya, Paulo ataŵalamula kukauza Silasi ndi Timoteyo kuti amlondole msanga. Paulo adaimirira pakati pa bwalo lija la Aeropagi nati: “Inu anthu aku Atene, pa zonse ndikuona kuti ndinu anthu opembedza kwambiri. Pakuti pamene ndidali kuyenda mu mzindamu, nkumaona malo anu osiyanasiyana achipembedzo, ndidapezanso guwa lina lansembe pamene padalembedwa mawu akuti: ‘Kwa Mulungu Wosadziŵika.’ Tsonotu amene mumampembedza osamdziŵayo, ndi yemweyo amene ine ndikukulalikirani. Mulungu amene adalenga dziko lapansi ndiponso zonse zili m’menemo, ndiye Mwini Kumwamba ndi dziko lapansi. Iye sakhala m’nyumba za chipembedzo zomangidwa ndi anthu ayi. Anthu sangamtumikire ndi manja awo, ngati kuti Iye amasoŵa kanthu. Pajatu Iye ndiye amapatsa anthu onse moyo, mpweya ndi zina zonse. Kuchokera mwa kholo limodzi Iye adalenga mitundu yonse ya anthu, kuti ikhale pa dziko lonse lapansi. Adakonzeratu nthaŵi ya moyo wawo, ndiponso malire a pokhala pawo. Mulungu adafuna kuti anthu amufunefune, ndipo kuti, pomfufuzafufuza, mwina nkumupeza. Komabe Iye sali kutali ndi aliyense mwa ife.
Paja: ‘Mwa Iye, ife timakhala ndi moyo, timayenda ndipo timakhala tilipo.’ Monga adanenera opeka ndakatulo anu ena kuti: ‘Ifenso ndife ofumira mwa Iye ngati ana ake.’ Tsono popeza kuti tili ngati ana a Mulungu, sitiyenera kuganiza kuti umulungu wake umafanafana ndi fano la golide, kapena la siliva kapena la mwala, lopangidwa mwa luso ndi nzeru za munthu. Mulungu adaŵalekerera anthu pa nthaŵi imene iwo adali osadziŵa, koma tsopano akuŵalamula anthu onse ponseponse kuti atembenuke mtima. Chifukwa adaika tsiku pamene Iye adzaweruza anthu apa dziko lonse lapansi molungama kudzera mwa Munthu amene Iye adamusankha. Adatsimikizira anthu onse zimenezi pakuukitsa Munthuyo kwa akufa.”
Pamene anthuwo adamva za kuuka kwa akufa, ena adangoseka. Koma ena adati: “Bwanji mudzatiuzenso zimenezi tsiku lina.” Choncho Paulo adaŵasiya. Koma ena adamutsata, nakhulupirira. Pakati pawo padali Diyoniziyo, mmodzi mwa a bwalo la milandu lotchedwa Areopagi, ndiponso mayi wina, dzina lake Damalisi, ndi enanso. Pambuyo pake Paulo adachoka ku Atene napita ku Korinto.
*Mau a Ambuye*
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 148: 1-2, 11-12, 13, 14
*Dziko lapansi ndi Kumwamba ladzaza ndi ulemu wanu*.
Tamandani Chauta inu okhala Kumwamba,
Mtamandeni inu okhala mlengalenga!
Mtamandeni inu anjelo ake onse,
Mtamandeni inu magulu a ankhondo ake onse!
*Dziko lapansi ndi Kumwamba ladzaza ndi ulemu wanu*.
Inu mafumu apa dziko lapansi, ndi anthu a mitundu yonse,
Inu akuluakulu ndi olamulira dziko lapansi!
Inu anyamata pamodzi ndi anamwali,
Inu okalamba ndi ana omwe!
*Dziko lapansi ndi Kumwamba ladzaza ndi ulemu wanu*.
Onsewo atamande dzina la Chauta,
Pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka,
Ulemerero wake ndi woposa,
Pansi pano ndi Kumwamba komwe.
*Dziko lapansi ndi Kumwamba ladzaza ndi ulemu wanu*.
Chauta wakweza anthu ake poŵapatsa mphamvu.
Walemekeza anthu ake onse oyera mtima,
Aisraele amene Iye amaŵakonda.
Tamandani Chauta!
*Dziko lapansi ndi Kumwamba ladzaza ndi ulemu wanu*.
*Aleluya*: (Yohane 14: 16) Ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthaŵi zonse, *Aleluya*.
*MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE 16:12-15*
Yesu adati kwa ophunzira ake: “Ndili nawo mawu ena ambiri oti ndikuuzeni, koma simungathe kuŵamvetsa tsopano ayi. Koma akadzafika Mzimu, wodziŵitsa choona uja, adzakuphunzitsani choona chonse. Pakuti sadzalankhula zochokera kwa Iye yekha ayi, koma ziri zonse zimene Atate adzamuuze, ndizo zimene adzalankhula. Ndipo adzakudziŵitsani zinthu za mtsogolo. Adzandilemekeza, pakuti adzatenga zochokera kwa Ine nadzakudziŵitsani. Zonse za Atate nzanga. Nchifukwa chake ndanena kuti adzatenga zochokera kwa Ine, nadzakudziŵitsani inu.”
*Mthenga wa Ambuye*